spot_img
16.9 C
New York
Tuesday, April 30, 2024
spot_img

A Chakwera vumbulukani, a Malawi akufuna mayankho– HRDC

Bungwe lomenyera ufulu wa anthu la HRDC lafunsa mtsogoleli wadziko lino Dr Lazarus Chakwera kuti abwere poyera ndikupeleka mayankho pa vuto la kusowa kwa mafuta m’dziko muno.

Kudzera mu kalata yomwe bungweri latulutsa, ati kukhalachete kwa mtsogoleli wa dziko lino pankhaniyi kukupereka chithunzithunzi chakuti dziko lino lilibe utsogoleri wothekera kubweretsa mayankho pa mavuto omwe nzika zake zikudutsamo.

Wachiwiri kwa wapampando bungweri a Michael Kaiyatsa atiwuza kuti ngati mtsogoleri wadziko lino sabwera poyera ndikupereka mayankho, chuma cha dziko lino chipitirira kulowa pansi ponena kuti malonda omwe amadalira mafutawa akulephera kuyenda..

Posachedwapa, bungwe la MERA linati vutoli lafika pamenepa kaamba kakusowa kwa ndalama zakunja zomwe dziko lino limafuna kuti liyitanitse mafuta kuchoka kunja kwa dziko lino.

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles