spot_img
16.7 C
New York
Friday, May 17, 2024
spot_img

Membala wa UTM alipira K5 million kaamba koluma mphuno ya membala wa MCP

Alick Saini, omwe ndi mtsogoleri wa chipani Cha UTM ku Kasungu awagamula kuti apeleke K5 050 000 ngati chindapusa atapezeka olakwa pa mlandu oluma ndi kudula mphuno ya mtsogoleri wa achinyamata a chipani cha MCP, a Chisomo Kefa.

A Saini adapalamula mlanduwu pa 1 September chaka chino atasemphana chichewa ndi a Kefa pa nkhani za pa chiweniweni.

Mwa ndalamazi K4.5 miliyoni ndi chipukuta misonzi chopitsa kwa Kefa pomwe K550,000 ndi yopita ku boma.

Asaini akuyenera kupereka K1.5 miliyoni kwa a Kefa komanso K550,000 ku boma lero kuti awamasule ndipo ndalama yotsalayo awapatsa miyezi isanu kuti amalize.

Magistrate Jones Masula wabwaloli wati wapereka chilangochi chifukwa zomwe adachita a Saini zidapereka chilema chamuyaya kwa a Kefa.

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles