spot_img
14.6 C
New York
Tuesday, May 14, 2024
spot_img

Atoht Manje wamwalira  

Mmodzi mwa oyimba chamba cha lokolo Atoht Manje wamwalira atadwala kwanthawi yochepa m’boma la Rumphi komwe amakayimba.

Malingana ndi Saint, mmodzi mwa oyimba omwe anali ndi oyimbayu usiku wathawu ku sukulu yaukachenjede ya Livingstonia ku Laws Campus wati Manje anayamba kudandaula kuti akumva kutentha atamaliza kuyimba pasukulupo kenako anakomoka.

Malipoti akusonyeza kuti pomwe amafika naye kuchipatala cha Livingstonia, oyimbayu anali atatisiya kale.

Manje amadziwika kwambiri ndi nyimbo monga Huwa, Zilibwino komanso Che-Patuma mwazina.-MBC

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles